Download PDF
Back to stories list

Tsiku lamene ndinanyamukira panyumba kuyenda kumzinda The day I left home for the city

Written by Lesley Koyi, Ursula Nafula

Illustrated by Brian Wambi

Translated by Jones Jere Joshua

Read by Christine Mwanza

Language Nyanja

Level Level 3

Narrate full story The audio for this story is currently not available.


Poimirira mabasi ag’ono kumudzi kwathu panali potanganidwa ndi mabasi olonga kwambiri. Pansi panalinso katundu oculuka ofunika kulongedwa. Oitanitsa anthuanali kufuula maina akumenemabasi amapita.

The small bus stop in my village was busy with people and overloaded buses. On the ground were even more things to load. Touts were shouting the names where their buses were going.


“Taunu! Tauni! Kupita kumadzulo!” Ndinamvera oitanitsa kufuula. Iyo ndiyo basi ndimafuna kukwera.

“City! City! Going west!” I heard a tout shouting. That was the bus I needed to catch.


Basi yakutauni inali pafupi kudzala,koma anthu ambirianali akali kukankha kuti alowe. Ena analonga katundu yao munsi mwa basi. Ena anaika moika katundu mkati mwa basi.

The city bus was almost full, but more people were still pushing to get on. Some packed their luggage under the bus. Others put theirs on the racks inside.


Okwera atsopano anagwira matikiti ao pomwe amafuna-funa pomwe angakhale mu basi yodzala ndi anthu. Azimai a ana ang’ono ang’ono anawakhazika bwino paulendo utali.

New passengers clutched their tickets as they looked for somewhere to sit in the crowded bus. Women with young children made them comfortable for the long journey.


Ndinaziika pafupi ndi dzenera. Munthu amena anakhala pafupi ndi ine anagwirira pulasitiki ya msipu. Anvala nkhwawilo zakale, khoti lakutha, ndipo amaoneka wamantha.

I squeezed in next to a window. The person sitting next to me was holding tightly to a green plastic bag. He wore old sandals, a worn out coat, and he looked nervous.


Ndinapenya kubwalo kwa basi ndipo ndinazindikira kuti ndinali kusiya mudzi wanga, kumalo komwe ndinakulira. Ndinali kupita ku tauni yaikulu.

I looked outside the bus and realised that I was leaving my village, the place where I had grown up. I was going to the big city.


Kulonga kunamalizika ndipo aulendo onse anakhazikika pansi. Azamalonda naonso anali kuzipatikiza kulowa mubasi kugulitsa katundu wao ku aulendo. Aliyense anali kufuula maina azomwe zinalipo zogulitsa. Mau anamveka odabwitsa kwa ine.

The loading was completed and all passengers were seated. Hawkers still pushed their way into the bus to sell their goods to the passengers. Everyone was shouting the names of what was available for sale. The words sounded funny to me.


Aulendo ang’ono anagulako zakumwa, ane anagulako zakudya zotsekemera za zing’ono zing’ono ndipo anayamba kutamfuna. Aja amene analibe ndalama, monga ine tinangopenyerera.

A few passengers bought drinks, others bought small snacks and began to chew. Those who did not have any money, like me, just watched.


Zocita zimenezi zinasokonezedwa ndi kulira kwa huta ya bus, kudziwitsa kuti tinali pafupi kunyamuka. Onenezera anafuulira ogulitsa kuti atuluke kubwalo.

These activities were interrupted by the hooting of the bus, a sign that we were ready to leave. The tout yelled at the hawkers to get out.


Ogulitsa anakankhana wina ndi mnzace kuti atuluke mu basi. Ena anali kupereka cenji kwa apaulendo. Ena amayesa kugulitsa zinthu zao nthawi yothera.

Hawkers pushed each other to make their way out of the bus. Some gave back change to the travellers. Others made last minute attempts to sell more items.


Pomwe basi imacoka pa sitesheni ya basi, ndinayangana padzenera. Ndinaganizira ngati ndizabweranso kumudzi wanga.

As the bus left the bus stop, I stared out of the window. I wondered if I would ever go back to my village again.


Pomwe ulendo umacitika, mkati mwa basi munatentha kwambiri. Ndinatseka maso anga kuyesa kugona.

As the journey progressed, the inside of the bus got very hot. I closed my eyes hoping to sleep.


Koma maganizo anabwereanso kumudzi. Kodi amai anga adzakhala bwino? Kodi akalulu anga azabweretsa ndalama zirizonse? Kodi mukulu wanga adzakumbukira kuthirira mbeu zanga zamitengo?

But my mind drifted back home. Will my mother be safe? Will my rabbits fetch any money? Will my brother remember to water my tree seedlings?


Mnjira, ndinakumbukira dzina ya malo amene amalume anakhalako mu tauni yakulu. Ndinali ndikali kung’ung’udzira pamene tulo tunanigwira ndipo ndinagona.

On the way, I memorised the name of the place where my uncle lived in the big city. I was still mumbling it when I fell asleep.


Maola asanundi anai atsatira, ndinauka ndi phokoso lalikulu ndi kuitana kwa apaulendo amubasi apita kumudzi kwanga. Ndinatenga cola canga cacing’ono ndi kulumphira kubwalo kwa basi.

Nine hours later, I woke up with loud banging and calling for passengers going back to my village. I grabbed my small bag and jumped out of the bus.


Basi yobwerera kumudzi imadzala mofulumira. Mosacedwa inayamba ulendo wopita kum’mawa. Cofunikira ceni-ceni kwa ine tsopano, cinali cakuyamba kufuna-funa nyumba ya amalume anga.

The return bus was filling up quickly. Soon it would make its way back east. The most important thing for me now, was to start looking for my uncle’s house.


Written by: Lesley Koyi, Ursula Nafula
Illustrated by: Brian Wambi
Translated by: Jones Jere Joshua
Read by: Christine Mwanza
Language: Nyanja
Level: Level 3
Source: The day I left home for the city from African Storybook
Creative Commons License
This work is licensed under a Creative Commons Attribution 4.0 International License.
Options
Back to stories list Download PDF